Mtendere
Anthu ambiri sasangalala ndi mtendere chifukwa chakuti ali kunja kwa chifuniro cha Mulungu. Iwo amatsata chifuniro chawo osati chifuniro cha Mulungu. Iwo amachita zimene akumvetsera ngati kapena kuganizira kuti ndi zolondola osati kutsatira Mau a Mulungu ndi kutsogozedwa ndi mtendere. Mwana aliyense wa Mulungu obadwanso kwa tsopano ayenera kumasangalala ndi moyo wodzazidwa ndi mtendere. Ngatitu inu mulibe mtendere simukusangalala ndi moyowu ai.